Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 22:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo mthenga anati, Usaike dzanja lako pa mwana, usamcitire iye kanthu; cifukwa tsopano ndidziwa kuti iwe umuopa Mulungu, pakuti sunandikanize ine mwana wako, mwana wako wayekha.

13. Ndipo Abrahamu anatukula maso ace nayang'ana taonani, pambuyo pace nkhosa yamphongo yogwiridwa ndi nyanga zace m'ciyangoyangomo; ndipo ananka Abrahamu nakatenga nkhosa yamphongoyo, naipereka nsembe yopsereza m'malo mwa mwana wace.

14. Ndipo Abrahamu anacha dzina lace la malowo Yehova-Yire: monga ati lero lomwe, M'phiri la Yehova cidzaoneka.

15. Ndipo mthenga wa Yehova anamuitana Abrahamu ndi mau odzera kumwamba kaciwiri,

16. nati, Pa Ine ndekha ndalumbira, ati Yehova, popeza wadta ici, sunandikaniza mwana wako, mwana wako wa yekha,

17. kudalitsa ndidzakudalitsa iwe, kucurukitsa ndidzacurukitsa mbeu zako monga nyenyezi za kumwamba, monga mcenga wa m'mphepete mwa nyanja; ndipo mbeu zako zidzagonjetsa cipata ca adani ao;

18. m'mbeu zako mitundu yonse ya dziko lap ansi idzadalitsidwa: cifukwa wamvera mau anga.

Werengani mutu wathunthu Genesis 22