Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 21:11-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo mauwo anaipira Abrahamu cifukwa ca mwana wace.

12. Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Usaipidwe nao, cifukwa ca mnyamatayo, ndi cifukwa ca mdzakazi wako; momwe monse akunenera iwe Sara umvere iwe mau ace; cifukwa kuti mwa Isake zidzaitanidwa mbeu zako.

13. Ndipo mwana wamwamuna wa mdzakazi uyo ndidzayesa mtundu, cifukwa iye ndiye mbeu yako.

14. Ndipo Abrahamu analawira m'mamawa, natenga mkate ndi mcenje wa madzi, nampatsa Hagara, naika paphewa pace, ndi mwana, namcotsa iye: ndipo iye anamuka, nasocerera m'cipululu ca Beereseba.

15. Ndipo anatha madzi a m'mcenje ndipo anaika mwana pansi pa citsamba.

16. Ndipo ananka nakhala pansi popenyana naye patari, monga pakugwa mubvi: cifukwa anati, Ndisaone kufa kwa mwana. Ndipo anakhala popenyana naye, nakweza mau ace nalira,

17. Ndipo Mulungu anamva mau a mnyamatayo, ndi mthenga wa Mulungu anamuitana Hagara, ndi mau odzera kumwamba, nati kwa iye, Watani Hagara? usaope; cifukwa Mulungu anamva mau a mnyamata kumene ali.

18. Tauka, nuukitse mnyamatayo, ndi kumgwira m'dzanja lako; cifukwa ndidzamuyesa iye mtundu waukuru.

19. Ndipo Mulungu anamtsegula m'maso mwace, ndipo anaona citsime ca madzi; namuka nadzaza mcenje ndi madzi, nampatsa mnyamata kuti amwe.

20. Ndipo Mulungu anakhala ndi mnyamata, ndipo anakula iye; nakhala m'cipululu, nakhala wauta.

21. Ndipo anakhala m'cipululu ca Parana; ndipo amace anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Aigupto.

22. Ndipo panali nthawi yomweyo. Abimeleke ndi Fikolo kazembe wa nkhondo yace anati kwa Abrahamu, kuti, Mulungu ali pamodzi ndi iwe m'zonse uzicita iwe;

23. tsopano iwe undilumbirire ine pano pa Mulungu kuti sudzandinyenga ine, kapena mwana wanga, kapena mdzukulu wanga: koma monga ufulu ndakucitira iwe udzandicitire ine, ndi dziko lomwe wakhalamo, ngati mlendo.

24. Ndipo Abrahamu anati, Ine ndidzalumbira.

Werengani mutu wathunthu Genesis 21