Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 17:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Koma za Ismayeli, ndamvera iwe: taona, ndamdalitsa iye, ndipo ndidzamcurukitsa iye ndithu; adzabala akaronga khumi ndi awiri, ndipo ndidzamuyesa iye mtundu waukuru.

21. Koma pangano langa ndidzalimbikitsa ndi Isake, amene Sara adzakubalira iwe nthawi yomwe yino caka camawa.

22. Ndipo analeka kunena naye, ndipo Mulungu anakwera kucokera kwa Abrahamu.

23. Ndipo Abrahamu anatenga Ismayeli mwana wace ndi onse amene anabadwa m'nyumba mwace, ndi onse, amene anagulidwa ndi ndalama zace, amuna onse a mwa anthu a kunyumba kwace kwa Abrahamu, nadula khungu lao tsiku lomwelo, monga Mulungu ananena naye.

Werengani mutu wathunthu Genesis 17