Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 13:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo anankabe ulendowace kucokera ku dziko la kumwera kunka ku Beteli, kufikira kumalo kumene kunali hema wace poyamba paja, pakati pa Beteli ndi Ai;

4. kumalo kwa guwa la nsembe analimanga iye kumeneko, poyamba paja; ndipo pamenepo Abramu anaitanira dzina la Yehova.

5. Ndiponso Loti anayenda ndi Abramu anali ndi nkhosa ndi ng'ombe ndi mahema.

6. Ndipo dziko silinathe kuwakwanira iwo, kuti akhale pamodzi: cifukwa kuti cuma cao cinali cambiri, ndipo sanathe kukhala pamodzi.

7. Ndipo panali ndeu, abusa a Abramu kudana ndi abusa a Loti: Akanani ndi Aperezi ndipo analinkukhala nthawi yomweyo m'dzikomo.

8. Ndipo Abramu anati kwa Loti, Tisacite ndeu, ine ndi iwe, abusa anga ndi abusa ako: cifukwa kuti ife ndife abale.

9. Dziko lonse siliri pamaso pako kodi? Ulekanetu ndi ine: ukanka iwe ku dzanja lamanzere, ine ndinka ku dzanja lamanja: ukanka iwe ku dzanja lamanja, ine ndinka ku dzanja lamanzere.

Werengani mutu wathunthu Genesis 13