Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 42:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo linga linali kunialo, loli'ngana ndi nyumba yazipinda, kuloza ku bwalo lakunja, popenyana ndi nyumba yazipinda, m'litali mwace munali mikono makumi asanu.

8. Pakuti kupingasa kwace kwa nyumba yazipinda inali m'bwalo lakunja, kunali mikono makumi asanu; ndipo taonani, kuloza ku khomo la Kacisi inali mikono zana limodzi.

9. Ndipo pansi pa zipinda izi panali polowera mbali ya kum'mawa, poloweramo kucoka ku bwalo lakunja.

10. M'kucindikira kwa linga la bwalo, kuloza kumwera, cakuno ca mpatawo, cakuno ca nyumba, panali nyumba yazipinda.

11. Ndipo njira ya pakhomo pao inanga maonekedwe a njira ya ku nyumba yazipinda yoloza kumpoto, inalingana nayo m'litali mwace, momwemonso kupingasa kwace; ndi m'maturukiro mwace monse munali monga mwa macitidwe a inzace, ndi monga mwa makomo a inzace.

12. Ndi monga mwa makomo a zipinda za kumwela panali khomo polekeza njira, ndiyo njira yokhudzana ndi linga la kum'mawa polowamo.

13. Pamenepo anati kwa ine, Zipinda za kumpoto, ndi zipinda za kumwela, ziri cakuno ca mpatawo, ndizo zipinda zopatulika, kumene ansembe okhala pafupi pa Yehova azidyera zinthu zopatulikitsa; kumeneko aziika zopatulikitsa, ndi nsembe yaufa, ndi nsembe yaucimo, ndi nsembe yoparamula; pakuti malowo ndi opatulika.

14. Atalowa ansembe asaturukenso m'malo opatulika kumka ku bwalo lakunja, koma komweko aziika zobvala zao zimene atumikira nazo; pakuti ziri zopatulika; ndipo abvale zobvala zina, nayandikire zinthu wamba za anthu.

15. Atatha tsono kuyesa nyumba ya m'katimo, anaturuka nane njira ya cipata coloza kum'mawa, nayesa bwalo pozungulira pace.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 42