Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 28:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Mwa mphulupulu zako zocuruka ndi malonda ako osalungama waipsa malo ako opatulika; cifukwa cace ndaturutsa moto m'kati mwako wakunyeketsa iwe; ndipo ndakusandutsa mapulusa panthaka pamaso pa onse akuona.

19. Onse akudziwa iwe mwa mitundu ya anthu adzadabwa nawe; wasanduka coopsa, ndipo sudzakhalanso konse.

20. Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,

21. Wobadwa ndi munthu iwe, lozetsa nkhope yako ku Zidoni, nuunenere;

22. uziti, Atero Ambuye Yehova, Taona, nditsutsana nawe Zidoni, ndipo ndidzalemekezedwa pakati pako; ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova pakucita Ine maweruzo mwa uwu, ndi kuzindikiridwa Woyera mwa uwu.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 28