Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 27:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Okhala m'Zidoni ndi Arivadi ndiwo opalasa ako; anzeru ako, Turo, okhala mwa iwe, ndiwo oongolera ako.

9. Akr-ru a ku Gebala ndi eni luso ace anali mwa iwe kukonza ziboo zako; zombo zonse za kunyanja pamodzi ndi amarinyero ao anali mwa iwe kusinthana nawe malonda.

10. Aperisiya, Aludi, Apuri, anali m'khamu lako; anthu ako a nkhondo anapacika cikopa ndi cisoti mwa iwe, anamveketsa kukoma kwako.

11. Anthu a Ativadi pamodzi ndi ankhondo ako anali pa malinga ako pozungulira, ndi Agamadi anali mu nsanja zako; anapacika zikopa zao pa makoma ako pozungulira, anakwaniritsa kukoma kwako.

12. Tarisi anagulana nawe malonda m'kucuruka kwa cuma ciri conse; anagula malonda ako ndi siliva ndi citsulo, seta ndi ntobvu.

13. Yavani, Tuba, Meseke, anagulana nawe malonda; ndi anthu amoyo ndi zotengera zamkuwa anagulana nawe malonda.

14. Iwo a nyumba ya Togarima anagula malonda ako ndi akavalo, ndi akavalo a nkhondo, ndi nyuru.

15. Anthu a ku Dedani anakutsatsa malonda, zisumbu zambiri zinazolowerana nawe malonda ako, anabwera nazo minyanga ndi phingo kugulana nawe malonda.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 27