Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 20:39-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo inu, nyumba ya Israyeli, atero Ambuye Yehova, mukani, tumikirani yense mafano ace, ndi m'tsogolo momwe, popeza simundimvera Ine; koma musaipsanso dzina langa lopatulika ndi zopereka zanu ndi mafano anu.

40. Pakuti pa phiri langa lopatulika, pa phiri lothubvuka la Israyeli, ati Ambuye Yehova, pomwepo onse a nyumba ya Israyeli, onsewo adzanditumikira Ine m'dzikomo; pomwepo ndidzawalandira, ndi pomwepo ndidzafuna nsembe zanu zokweza, ndi zoyamba za msonkho wanu, pamodzi ndi zopatulika zanu zonse.

41. Ngati pfungo lokoma ndidzakulandirani pakukuturutsani mwa mitundu ya anthu, ndipo ndidzakusonkhanitsani kukucotsani m'maiko munabalalikiramo, ndipo ndidzazindikirika Woyera mwa inu pamaso pa amitundu.

42. Ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakukulowetsani Ine m'dzil ko la Israyeli, m'dzikoli ndinalikwezera dzanja langa kulipereka kwa makolo anu.

43. Ndi pomwepo mudzakumbukila njira zanu, ndi zonse mudazicita ndi kudzidetsa nazo, ndipo mudzakhala onyansa pamaso pa inu nokha, cifukwa ca zoipa zanu zonse mudazicita.

44. M'mwemo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova nditacita nanu cifukwa ca dzina langa, si monga mwa njira zanu zoipa, kapena monga mwa macitidwe anu obvunda, nyumba ya Israyeli inu, ati Ambuye Yehova.

45. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 20