Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 16:44-55 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Taona, ali yense wonena miyambi adzakunenera mwambi uwu, wakuti, Monga mace momwemo mwana wace.

45. Iwe ndiwe mwana wa mako wonyansidwa naye mwamuna wace ndi ana ace, ndipo iwe ndiwe mng'ono wao wa akulu ako akunyansidwa ndi amuna ao ndi ana ao; mai wako ndiye Mhiti, ndi atate wako ndiye M-amori.

46. Ndi mkulu wako ndiye Samariya, wokhala ku dzanja lako lamanzere, iye ndi ana ace akazi; ndi mng'ono wako wokhala ku dzanja lako lamanja ndiye Sodomu ndi ana ace akazi.

47. Koma sunayenda m'njira zao, kapena kucita monga mwa zonyansa zao pang'ono pokha; unawaposa iwo m'kubvunda kwako, m'njira zako zonse.

48. Pali ine, ati Ambuye Yehova, Sodomu mng'ono wako sanacita, iye kapena ana ace akazi, monga umo unacitira iwe ndi ana ako akazi.

49. Taona, mphulupulu ya mng'onowako Sodomu ndi iye, kudzikuza, kucuruka kwa cakudya, ndi kupumula kwa mtambasali, anali nako iye ndi ana ace; ndipo sanalimbitsa dzanja la wosauka ndi wosowa.

50. Ndipo anadzikuza, nacita conyansa pamaso panga; cifukwa cace ndinawacotsa pakuciona.

51. Ngakhale Samariya sanacita theka la zocimwa zako, koma unacurukitsa zonyansa zako kuwaposa iwowa, ndi kuika abale ako olungama ndi zonyansa zako zonse unazicita.

52. Usenzenso manyazi ako, iwe wakuweruza abale ako mwa zocimwa zako unazicita monyansa koposa iwowa; iwo akuposa iwe m'cilungamo cao, nawenso ucite manyazi nusenze manyazi ako, popeza waika abale ako olungama.

53. Ndipo ndidzabweza undende wao, undende wa Sodomu ndi ana ace, ndi undende wa Samariya ndi ana ace, ndi undede wa andende ako pakati pao;

54. kuti usenze manyazi ako, ndi kuti ucite manyazi cifukwa ca zonse unazicita pakuwatonthoza.

55. Ndipo abale ako Sodomu ndi ana ace adzabwerera umo unakhalira kale; ndi iwe ndi ana ako mudzabwerera umo munakhalira kale.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 16