Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezekieli 1:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Poyenda zija zinayenda izi, poima zija zinaima izi; ndipo ponyamuka pansi zija njingazi zinanyamuka pambali pa izo; pakuti mzimu wa zamoyozo unali mu njingazi.

22. Ndi pa mitu ya zamoyozi panali cifaniziro ca thambo, monga mawalidwe a krustalo woopsa, loyalika pamwamba pamitu pao.

23. Ndi pansi pa thambolo mapiko ao analunjikana, lina kulunjika ku linzace; ciri conse cinali nao mapiko awiri akuphimba matupi ao, cakuno ndi cauko.

24. Ndipo pakuyenda izi ndinamva mkokomo wa mapiko ao, ngati mkokomo wa madzi akulu, ngati mau a Wamphamvuyonse, phokoso lakusokosera ngati phokoso la ankhondo; pakuima zinagwetsa mapiko ao.

25. Ndipo panamveka mau pamwamba pa thambolo linali pamwamba pa mitu yao; pakuima izi zinagwetsa mapiko ao.

26. Ndi pamwamba pa thambo linali pamitu pao panali cifaniziro ca mpando wacifumu, maonekedwe ace ngati mwala wa safiro; ndipo pa cifaniziro ca mpando wacifumu panali cifaniziro ngati maonekedwe ace a munthu wokhala pamwamba pace.

Werengani mutu wathunthu Ezekieli 1