1. Pakupemphera Ezara tsono, ndi kuulula ndi kulira misozi, ndi kudzigwetsa pansi pakhomo pa nyumba ya Mulungu, udamsonkhanira mwa Israyeli msonkhano waukuru ndithu wa amuna, ndi akazi, ndi ana; popeza anthu analira kulira, kwakukuru.
2. Pamenepo Sekaniya mwana wa Yehiyeli, mwana wina wa Elamu, anambwezera Ezara mau, nati, Talakwira Mulungu wathu, tadzitengera akazi acilendo a mitundu ya dzikoli; koma tsopano cimtsalira Israyeli ciyembekezo kunena za cinthu ici.