Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Estere 9:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwezi wakhumi ndi ciwiri tsono, ndiwo mwezi wa Adara, tsiku lace lakhumi ndi citatu, mau a mfumu ndi lamulo lace ali pafupi kucitika, tsikuli adani a Ayuda anayesa kuwacitira ufumu, koma cinasinthika; popeza Ayuda anacitira ufumu iwo odana nao;

2. pakuti Ayuda anasonkhana pamodzi m'midzi mwao, m'maiko onse a mfumu Ahaswero, kuwathira manja ofuna kuwacitira coipa, ndipo palibe munthu analimbika pamaso pao; popeza kuopsa kwao kudawagwera mitundu yonse ya anthu.

3. Ndipo akalonga onse a maikowo, ndi akazembe, ndi ziwanga, ndi iwo ocita nchito ya mfumu, anathandiza Ayuda; popeza kuopsa kwa Moredekai kudawagwera.

4. Pakuti Moredekai anali wamkuru m'nyumba ya mfumu, ndi mbiri yace idabuka m'maiko onse; pa kuti munthuyu Moredekai anakula-kulabe.

5. Ndipo Ayuda anakantha adani ao onse, kuwakantha ndi lupanga, ndi kuwapulula, nacitira odana nao monga anafuna.

6. Ndipo m'cinyumba ca ku Susani Ayuda anakantha, naononga amuna mazana asanu.

7. Napha Parisandata, ndi Dalifoni, ndi Asipata,

8. ndi Porata, ndi Adaliya, ndi Aridata,

9. ndi Parimasta, ndi Arisai, ndi Aridai, ndi Vaisata,

10. ana amuna khumi a Hamani mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalanda zofunkha.

11. Tsiku lomwelo anabwera naco kwa mfumu ciwerengo ca iwo ophedwa m'cinyumba ca ku Susani.

12. Ndipo mfumu inati kwa mkazi wamkuru Estere, Ayuda adapha, naononga amuna mazana asanu m'cinyumba ca ku Susani, ndi ana amuna khumi a Hamani; nanga m'maiko ena a mfumu munacitikanji? pempho lanu ndi ciani tsono? lidzacitikira inu; kapena mufunanjinso? kudzacitika.

Werengani mutu wathunthu Estere 9