Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 8:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakuti ukapanda kulola anthu anga amuke, taona, ndidzatuma mizaza pa iwe, ndi pa anyamata ako, ndi pa anthu ako, ndi pa nyumba zako; ndipo nyumba za Aaigupto zidzadzala nayo mizaza, ndi nthaka yomwe imene ikhalapo.

22. Ndipo tsiku ilo ndidzalemba malire dziko la Goseni, m'mene mukhala anthu anga, kuti pamenepo pasakhale mizaza; kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova pakati pa dzikoli.

23. Ndipo ndidzaika cosiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako; mawa padzakhala cizindikilo ici.

24. Ndipo Yehovaanacita comweco; ndipo kunafika magulu a mizaza m'nyumba ya Farao, ndi m'nyumba za anyamata ace, ndi m'dziko lonse la Aigupto; dziko linaipatu cifukwa ca mizazayo.

25. Pamenepo Farao anaitana Mose ndi Aroni, nati, Mukani, mphereni nsembe Mulungu wanu m'dzikomu.

26. Koma Mose anati, Sikuyenera kutero; pakuti tidzamphera Yehova Mulungu wathu conyansa ca Aaigupto; taonani, ngati tikamphera nsembeconyansaca Aaigupto pamaso pao sadzatiponya miyala kodi?

Werengani mutu wathunthu Eksodo 8