Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 4:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo kudzatero, aka panda kukhulupirira zingakhale zizindikilo izi, ndi kusamvera mau ako, ukatunge madzi a kunyanja, ndi kuthira pamtunda; ndi madzi watunga ku nyanjayo adzasanduka mwazi pamtunda.

10. Ndipo Mose anati kwa Yehova, Mverani, Ambuye, ine ndine munthu wosowa ponena, kapena dzulo, kapena kale, kapena cilankhulire Inu ndi kapolo wanu, pakuti ndine wa m'kamwa molemera, ndi wa lilime lolemera.

11. Koma Yehova ananena naye, Anampangira munthu m'kamwa ndani? Kapena analenga munthu wosalankhula ndani, kapena wogontha, kapena wamaso, kapena wakhungu? Si ndine Yehova kodi?

12. Ndipo tsopano muka, ndipo Ine ndidzakhala m'kamwa mwako, ndi kukuphunzitsa comwe ukalankhule.

13. Koma anati, Mverani, Ambuye, tumizani pa dzanja la iye amene mudzamtuma.

14. Pamenepo mkwiyo wa Yehova unamyakira Mose, ndipo anati, Nanga Aroni Mlevi mbale wako sialipo kodi? Ndidziwa kuti kulankhula alankhula. Ndipo, taona, aturuka kudzakomana ndiwe; ndipo pakuona iwe adzakondweram'mtima mwace.

15. Ndipo ukalankhule naye, ndi kumpangira mau; ndipo Ine ndidzakhala m'kamwa mwako, ndi m'kamwa mwace, ndipo ndidzakuphunzitsani inu cimene mukacite.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 4