Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:19-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa nsonga ziwiri za capacifuwa, m'mphepete mwace m'katimo, pa mbali ya kuefodi.

20. Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa zapamapewa ziwiri za efodi pansi pace, pa mbali yace ya kutsogolo, pafupi pa msoko wace, pamwamba pa mpango wa efodi.

21. Ndipo anamanga capacifuwa pa mphete zace ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti cikhale pa mpango wa efodi, ndi kuti capacifuwa cisamasuke paefodi; monga Yehova anamuuza Mose.

22. Ndipo anaomba mwinjiro wa efodi, nchito yoomba ya lamadzi lokha;

23. ndi pakati pace polowa mutu, ngati polowa pa maraya ocingirizira, ndipo anabinyira pozungulira polowa pace, pangang'ambike.

24. Napangira pa mkawo wa mwinjiro makangaza a lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

25. Ndipo anapanga miriu ya golidi woona, napakiza miriu ndi makangaza, pa mkawo wa mwinjiro pozungulira, popakiza ndi makangaza.

26. Mliu ndi khangaza, mliu ndi khangaza pa mkawo wa mwinjiro pozungulira, kutumikira nazo; monga Yehova anamuuza Mose.

27. Ndipo anaomba maraya a bafuta, a nchito yoomba, a Aroni, ndi a ana ace amuna,

28. ndi nduwira va bafuta wa thonje losansitsa, ndi akapal okometsetsa a bafuta wa thonje losansitsa, ndi zobvala za kumiyendo za bafuta wa thonje losansitsa,

29. ndi mpango wabafuta wa thonje losansitsa, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, nchito ya wopikula; monga Yehova adamuuza Mose.

30. Ndipo anapanga phanthiphanthi wa korona wopatulika wa golidi woona, nalembapo lemba, ngati malocedwe a cosindikizira, KUPATULIKIRA YEHOVA.

31. Namangako mkuzi wamadzi, kuumanga nao pamwamba pa nduwira; monga Yehova adamuuza Mose.

32. Potero anatsiriza nchito yonseya kacisi wa cihema cokomanako; ndipo ana a Israyeli adacita monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, anacita momwemo.

33. Ndipo anabwera naye kacisi kwa Mose, cihemaco, ndi zipangizo zace zonse, zokowera zace, matabwa ace, mitanda yace, ndi mizati yace, nsanamira zace ndi nsici zace, ndi makamwa ace;

34. ndi cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiirira, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi nsaru yocinga yotsekera;

35. likasa la mboni, ndi mphiko zace, ndi cotetezerapo;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39