Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndi mzere waciwiri wa nofeki, safiri, ndi yahalomu.

12. Ndi mzere wacitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama.

13. Ndi mzere wacinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; inakhala yogwirika ndi golidi maikidwe ace.

14. Ndipo miyalayi inakhala monga mwa maina a ana a Israyeli, khumi ndi awiri, monga mwa maina ao; ngati malocedwe a cosindikizira, yonse monga mwa maina ace, kwa mafuko khumi ndi awiriwo.

15. Ndipo anapangira pacapacifuwa maunyolo ngati zingwe, nchito yopota ya golidi woona.

16. Anapanganso zoikamo ziwiri zagolidi, ndi mphete ziwiri zagolidi; naika mphete ziwirizo pa nsonga ziwiri za capacifuwa.

17. Ndipo anamanga maunyolo awiri opota agolidi pa mphete ziwiri pa nsonga za capacifuwa.

18. Ndi nsonga zace ziwiri zina za maunyolo awiri opotawo anazimanga pa zoikamo ziwiri, nazimanga pa zapamapewa za efodi, m'tsogolo mwace.

19. Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa nsonga ziwiri za capacifuwa, m'mphepete mwace m'katimo, pa mbali ya kuefodi.

20. Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa zapamapewa ziwiri za efodi pansi pace, pa mbali yace ya kutsogolo, pafupi pa msoko wace, pamwamba pa mpango wa efodi.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39