Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 36:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo aluso onse, akucita nchito yonse ya malo opatulika, anadza onse ndi kusiya nchito yao: analinkucita;

5. nanena ndi Mose, ndi kuti, Anthu alinkubwera nazo zocuruka, zakuposera zoyenera nchito imene Yehova anauza icitike.

6. Ndipo Mose analamulira, ndipo anamveketsa mau mwa cigono conse, ndi kuti, Asaonjezere nchito ya ku copereka ca malo opatulika, ngakhale mwamuna ngakhale mkazi. Tero anawaletsa anthu asabwere nazo zina.

7. Popeza zipangizo zinakwanira nchito yonse icitike, zinatsalakonso.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 36