Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 3:10-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Tiye tsopano, ndikutuma kwa Farao, kuti uturutse anthu anga, ana a Israyeli m'Aigupto.

11. Koma Mose anati kwa Mulungu, Ndine yani ine kuti ndipite kwa Farao, ndi kuti nditurutse ana a Israyeli m'Aigupto?

12. Ndipo iye anati, Ine ndidzakhala ndi iwe; ndipo ici ndi cizindikilo ca iwe, cakuti ndakutuma ndine; utaturutsa anthuwo m'Aigupto mudzatumikira Mulungu paphiri pano.

13. Ndipo Mose anati kwa Mulungu, Onani, pakufika ine kwa ana a Israyeli, ndi kunena nao, Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu; ndipo akakanena ndi ine, Dzina lace ndani? ndikanena nao ciani?

14. Ndipo Molungu anati kwa Mose, INE NDINE YEMWE NDIRI INE. Anatinso, Ukatero ndi ana a Israyeli, INE NDINE wandituma kwa inu.

15. Ndipo Mulungu ananenanso kwa Mose, Ukatero ndi ana a Israyeli, Yehova, Molungu wa makolo anu, Molungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Molungu wa Yakobo anandituma kwa inu; ili nw dzina langa nthawi yosatha, ici ndi cikumbukiro canga m'mibadwo mibadwo.

16. Muka, nukasonkhanitse akuru a Israyeli, nunene nao, Yehova, Mulungu wa makolo anu anandionekera ine, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, ndi kuti; Ndakuzondani ndithu, ndi kuona comwe akucitirani m'Aigupto;

17. ndipo ndanena, Ndidzakukwezani kukuturutsani m'mazunzo a Aigupto, kukulowezani m'dziko la Akanani, ndi Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

18. Ndipo adzamveca mau ako; ndipo ukapite iwe ndi akuru a Israyeli, kwa mfumu ya Aigupto, ndi kukanena naye, Yehova, Mulungu wa Ahebri wakomana ndi ife; tiloleni, timuke tsopano ulendo wa masiku atatu m'cipululu, kuti timphere nsembe Yehova Mulungu wathu.

19. Koma Ine ndidziwa kuti mfumu ya Aigupto siidzalola inu kumuka, inde lingakhale ndi dzanja lamphamvu ai.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 3