Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 28:33-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Ndipo pa mbinyiru wace upange makangaza a lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiirira, pambinyiru pace pozungulira, ndi kuwapakiza ndi miliu yagolidi pozungulira;

34. mliu wagolidi ndi khangaza, mliu wagolidi ndi khangaza, pa mbinyiru wa mwinjiro pozungulira.

35. Ndipo Aroni aubvale kuti atumikire nao; ndipo limveke liu lace pakulowa iye m'malo opatulika pamaso pa Yehova, ndi pakuturuka iye, kuti asafe.

36. Ndipo upange golidi waphanthiphanthi woona, ndi kulocapo, monga malocedwe a cosindikizira. KUPATULIKIRA YEHOVA.

37. Nuciike pamkuzi wamadzi, ndipo cikhale panduwira, cikhale patsogolo pace pa nduwira.

38. Ndipo cizikhala pamphumi pace pa Aroni, ndipo Aroni azinyamula mphulupulu ya zopatulidwa, zimene ana a Israyeli azipatulira, ndi zopereka zao zonse zopatulira; ndipo cizikhala pamphumi pace kosalekeza, kuti alandiridwe pamaso pa Yehova.

39. Ndipo upikule maraya am'kati abafuta a thonje losansitsa, nusoke nduwira wabafuta, nusokenso mpango wopikapika.

40. Ndipo usokere ana a Aroni maraya am'kati, nuwasokere mipango; uwasokerenso akapa akhale aulemerero ndi okoma.

41. Ndipo ubveke nazo Aroni mbale wako, ndi ana ace omwe; ndi a kuwadzoza, ndi kudzaza dzanja lao, ndi kuwapatula, andicitire Ine nchito ya nsembe.

42. Uwasokerenso zobvala za miyendo za bafuta wa thome losansitsa kubisa marisece ao; ziyambire m'cuuno zifikire kuncafu.

43. Ndipo azibvale Aroni, ndi ana ace, pakulowa iwo ku cihema cokomanako, kapena poyandikiza iwo ku guwa la nsembe kutumikira m'malo opatulika; anganyamule mphulupulu, nangafe; likhale lemba losatha la iye ndi mbumba zace pambuyo pace.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 28