Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 2:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anamuka munthu wa banja la Levi, natenga mwana wamkazi wa Levi.

2. Ndipo anaima mkaziyo, naonamwanawamwamuna; m'mene anamuona kuti ali wokoma, anambisa miyezi itatu.

3. Koma pamene sanathe kumbisanso, anamtengera kabokosi kagumbwa, napakapo nkhunga ndi phula; naikamo mwanayo, nakaika pakati pa mabango m'mbali mwa nyanja.

4. Ndipo mlongo wace anaima patali, adziwe comwe adzamcitira.

5. Ndipo mwana wamkazi wa Farao anatsikira kukasamba m'nyanja; ndipo atsikana ace anayendayenda m'mbali mwa nyanja; ndipo iye anaona kabokosi pakati pa mabango, natuma mdzakazi wace akatenge.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 2