Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 18:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo kunatero kuti m'mawa mwace Mose anakhala pansi kuweruzira anthu mirandu yao; ndipo anthu anakhala ciriri pamaso pa Mose kuyambira m'mawa kufikira madzulo.

14. Ndipo pamene mpongozi wace wa Mose anaona zonsezi iye anawacitira anthu, anati, Cinthu ici nciani uwacitira anthuci? Umakhala pa wekha bwanji, ndi anthu onse amakhala ciriri pamaso pako kuyambira m'mawa kufikira madzulo?

15. Ndipo Moce anati kwa mpongozi wace, Cifukwa anthu amadza kwa ine kudzafunsira Mulungu;

16. akakhala nao mlandu adza kwa ine, kuti ndiweruze pakati pa munthu ndi mnansi wace, ndi kuti ndiwadziwitsemalemba a Mulungu, ndi malamulo ace.

17. Koma mpongozi wa Mose ananena naye, Cinthu ucitaci siciri cabwino ai.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 18