Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 15:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Mitundu ya anthu idamva, inanthunthumira;Kuda mtima kwagwira anthu okhala m'Filistiya.

15. Pamenepo mafumu a Edomu anadabwa;Agwidwa nako kunthunthumira amphamvu a ku Moabu;Okhala m'Kanani onse asungunukamtima.

16. Kuopa kwakukuru ndi mantha ziwagwera;Pa dzanja lanu lalikuru akhala cete ngati mwala;Kufikira apita anthu anu, Yehova,Kufikira apita anthu amene mudawaombola.

17. Mudzawafikitsa, ndi kuwaoka pa phiri la colowa canu,Pamalo pamene munadzipangira mukhalepo, Yehova,Malo oyera, amene manja anu, Ambuye, adakhazikika.

18. Yehova adzacita ufumu nthawi yomka muyaya.

19. Pakuti akavalo a Farao analowa m'nyanja, ndi magareta ace ndi apakavalo ace, ndipo Yehova anawabwezera madzi a m'nyanja; koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja.

20. Ndipo Miriamu mneneriyo, mlongo wa Aroni, anagwira lingaka m'dzanja lace; ndipo akazi onse anaturuka kumtsata ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe.

21. Ndipo Miriamu anawayankha,Yimbirani Yehova, pakuti wapambanatu;Kavalo ndi wokwera wace anawaponya m'nyanja.Madzi a ku Mara.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 15