Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 11:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Watsala moo umodzi ndidzamtengera Farao, ndi Aigupto; pambuyo pace adzakulolani mucoke kuno; pamene akulolani kupita, zoonadi adzakuingitsani kuno konse.

2. Lankhula tsopano m'makutu a anthu, kuti mwamuna yense apemphe kwa mnzace, ndi mkazi yense kwa mnzace, zokometsera zasiliva ndi zagolidi.

3. Ndipo Yehova anawapatsa anthu cisomo pamaso pa Aaigupto. Munthuyo Mose ndiyenso wamkuru ndithu m'dziko la Aigupto, pamaso pa anyamata a Farao, ndi pamaso pa anthu.

4. Ndipo Mose anati, Atero Yehova, Monga pakati pa usiku ndidzaturuka loe kumka pakati pa Aigupto;

5. ndipo ana onse oyamba a m'dziko la Aigupto adzafa, kuyambira mwana woyamba wa Farao wokhala pa mpando wacifumu wace, kufikira mwana woyamba wa mdzakazi wokhala pa miyala yopera; ndi ana onse oyamba a zoweta.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 11