Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 6:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. kuti muope Yehova Mulungu wanu, kusunga malemba ace onse ndi malamulo ace, amene ndikuuzani inu ndi ana anu, ndi zidzukulu zanu, masiku onse a moyo wanu, ndi kuti masiku anu acuruke.

3. Potero imvani, Israyeli, musamalire kuwacita, kuti cikukomereni ndi kuti mucuruke cicurukire, monga Yehova Mulungu wa makolo anu anena ndi inu, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

4. Imvani, Israyeli; Yehova Mulungu wathu, Yehova ndiye mmodzi;

5. ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.

6. Ndipo mau awa ndikuuzanilero, azikhala pamtima panu;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 6