Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 5:14-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. koma tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata la Yehova Mulungu wako; usamagwira nchito iri yonse, iwe, kapena mwana wako wamwamuna, kapena mwana wako wamkazi, kapena wanchito wako wamwamuna, kapena wanchito wako wamkazi, kapena ng'ombe yako, kapena buru wako, kapena zoweta zako ziri zonse, kapena mlendo wokhala m'mudzi mwako; kuti wanchito wako wamwamuna ndi wanchito wako wamkazi apumule monga iwe mwini.

15. Ndipo uzikumbukilakuti unali kapolo m'dziko la Aigupto, ndi kuti Yehova Mulungu wako anakuturutsako ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka; cifukwa cace Yehova Mulungu wako anakulamulira kusunga tsiku la Sabata.

16. Lemekeza atate wako ndi amako, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira; kuti masiku ako acuruke, ndi kuti cikukomere, m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.

17. Usaphe.

18. Usacite cigololo.

19. Usabe.

20. Usamnamizire mnzako.

21. Usasirire mkazi wace wa mnzako; usakhumbe nyumba yace ya mnzako, munda wace, kapena wanchito wace wamwamuna, kapena wanchito wace wamkazi, ng'ombe yace, kapena buru wace, kapena kanthu kali konse ka mnzako.

22. Yehova ananena mau awa kwa msonkhano wanu wonse, m'phirimo ali pakati pa moto, pamtambo, pamdima bii, ndi mau akuru; osaonjezapo kanthu. Ndipo anawalembera pa magome awiri amiyala, nandipatsa awa.

23. Ndipo kunali, pamene munamva liu loturuka pakati pa mdima, potentha phiri ndi moto, munayandikiza kwa ine, ndiwo mafumu onse a mapfuko anu ndi akuru anu;

24. ndipo munati, Taonani, Yehova Mulungu wathu anationetsa ulemerero wace, ndi ukuru wace, ndipo tidamva liu lace ali pakati pa mote; tapenya lero lino kuti Mulungu anena ndi munthu, ndipo akhala ndi moyo.

25. Ndipo tsopano tiferenji? popeza mote waukuru uwu udzatitha. Tikaonjeza kumva mau a Yehova Mulungu wathu, tidzafa.

26. Pakuti ndaniyo, wa zamoyo zonse adamva mau a Mulungu wamoyo wakunena ali pakati pa moto, monga ife, nakhala ndi moyo?

27. Yandikizani inu, ndi kumva zonse Yehova Mulungu wathu adzati; ndipo inu munene ndi ife zonse zimene Yehova Mulungu wathu adzanena ndi inu; ndipo ife tidzazimva ndi kuzicita.

28. Ndipo Yehova anamva mau a kunena kwanu, pamene munanena ndi ine; ndipo Yehova anati kwa ine, Ndidamva mau a kunena kwao kwa anthu awa, amene ananena ndi iwe; cokoma cokha cokha adanenaci.

29. Ha! mwenzi akadakhala nao mtima wotere wakundiopa Ine, ndi kusunga malamulo anga masiku onse, kuti ciwakomere iwo ndi ana ao nthawi zonse!

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 5