Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo ndinauza Yoswa muja, ndi kuti, Maso ako anapenya zonse Yehova Mulungu wanu anawacitira mafumu awa awiri; momwemo Yehova adzacitira maufumu onse kumene muolokerako.

22. Musawaopa popeza Yehova Mulungu wanu, ndiye agwirira inu nkhondo.

23. Ndipo ndinapempha cifundo kwa Yehova nthawi yomwe ija, ndi kuti,

24. Ambuye Yehova, mwayamba Inu kuonetsera mtumiki wanu ukulu wanu, ndi dzanja lanu lamphamvu; pakuti Mulungu ndani m'mwamba kapena pa dziko lapansi wakucita monga mwa nchito zanu, ndi monga mwa mphamvu zanu?

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3