Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Koma akazi anu, ndi ana anu, ndi zoweta zanu, (ndidziwa muli nazo zoweta zambiri), zikhale m'midzi yanu imene ndinakupatsani;

20. kufikira Yehova atapumulitsa abale anu, monga anapumulitsa inu, nalandira iwonso dziko limene Yehova Mulungu wanu awapatsa tsidya lila la Yordano; pamenepo mudzabwerera munthu yense ku colowa cace, cimene ndinakupatsani.

21. Ndipo ndinauza Yoswa muja, ndi kuti, Maso ako anapenya zonse Yehova Mulungu wanu anawacitira mafumu awa awiri; momwemo Yehova adzacitira maufumu onse kumene muolokerako.

22. Musawaopa popeza Yehova Mulungu wanu, ndiye agwirira inu nkhondo.

23. Ndipo ndinapempha cifundo kwa Yehova nthawi yomwe ija, ndi kuti,

24. Ambuye Yehova, mwayamba Inu kuonetsera mtumiki wanu ukulu wanu, ndi dzanja lanu lamphamvu; pakuti Mulungu ndani m'mwamba kapena pa dziko lapansi wakucita monga mwa nchito zanu, ndi monga mwa mphamvu zanu?

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3