Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 24:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Munthu akatenga mkazi akhale wace, kudzali, ngati sapeza ufulu pamaso pace, popeza anapeza mwa iye kanthu kosayenera, amlembere kalata wa cilekanitso, ndi kumpereka uyu m'dzanja lace, ndi kumturutsa m'nyumba mwace.

2. Ndipo ataturuka m'nyumba mwace, amuke nakhale mkazi wa mwamuna wina.

3. Ndipo akamuda mwamuna waciwiriyo, nakamlemberanso kalata wa cilekanitso, ndi kumpereka uyu m'dzanja lace, nakamturutsa m'nyumba mwace; kapena akamwalira mwamuna wotsirizayo, amene anamtenga akhale mkazi wace;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 24