Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 2:10-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. (Aemi anakhalamo kale, ndiwo anthu akuru, ndi ambiri, ndi atalitali, ngati Aanaki.

11. Anawayesa iwonso Arefai, monga Aanaki; koma Amoabu awacha Aemi.

12. Ndipo Ahori anakhala m'Seiri kale, koma ana a Esau analanda dziko lao, nawaononga pamaso pao, nakhala m'malo mwao; monga Israyeli anacitira dziko lace lace, limene Yehova anampatsa.)

13. Ukani tsopano, olokani mtsinje wa Zeredi. Ndipo tinaoloka mtsinje wa Zeredi.

14. Ndipo masiku amene tinayenda kucokera ku Kadesi Barinea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'cigono, monga Yehova adawalumbirira.

15. Komanso dzanja la Yehova linatsutsana nao, kuwaononga m'cigono, kufikira adawatha.

16. Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,

17. Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,

18. Lero lomwe utumphe malire a Moabu, ndiwo Ari.

19. Ndipo pamene uyandikiza popenyana ndi ana a Amoni, usawabvuta, kapena kuutsana nao; popeza sindidzakupatsako dziko la ana a Amoni likhale lako lako; popeza ndinapatsa ana a Loti ili likhale lao lao.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 2