Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 15:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Musamayesa neosautsa, pomlola akucokereni waufulu; popeza anakugwirirani nchito zaka zisanu ndi cimodzi monga wolipidwa wakulandira cowirikiza; potero Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m'zonse muzicita.

19. Zazimuna zonse zoyamba kubadwa, zobadwa mwa ng'ombe zanu ndi mwa nkhosa ndi mbuzi zanu, muzizipatulira Yehova Mulungu wanu; musamagwiritsa nchito yoyamba kubadwa mwa ng'ombe zanu, kapena kusenga yoyamba kubadwa ya nkhosa kapena mbuzi zanu.

20. Muzidye caka ndi caka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m'malo amene Yehova adzasankha, inu ndi a m'banja mwanu.

21. Koma ikakhala naco cirema, yotsimphina, kapena yakhungu, cirema ciri conse coipa, musamaiphera nsembe Yehova Mulungu wanu.

22. Muidye m'mudzi mwanu; odetsa ndi oyera aidye cimodzimodzi, monga mphoyo ndi nswala.

23. Mwazi wace wokha musamadya; muuthire pansi ngati madzi.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 15