Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 12:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Awa ndi malemba ndi maweruzo, muziwasamalirawa kuwacita m'dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani likhale lanu lanu, masiku onse akukhala ndi moyo inu pa dziko lapansi.

2. Muononge konse malo onse, amitundu amene mudzawalanda anatumikirako milungu yao, pa mapiri atali, ndi pa zitunda, ndi pansi pa mitengo yonse yabiriwiri;

3. nimugumule maguwa ao a nsembe, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kutentha zifanizo zao, ndi kulikha mafano osema a milungu yao; ndipo muononge dzina lao licoke m'malomo.

4. Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 12