Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 9:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kubvomereza, ndi kuti, Ambuye Mulungu wamkuru ndi woopsa, wakuwasungira pangano ndi cifundo iwo akukukondani, ndi kusunga malamulo anu,

5. tacimwa, tacita mphulupulu, tacita zoipa, tapanduka, kupambuka ndi kusiya maneno anu ndi maweruzo anu;

6. sitinamvera atumiki anu aneneri, amene ananena m'dzina lanu kwa mafumu athu, akalonga athu, makolo athu, ndi anthu onse a m'dziko.

7. Ambuye, cilungamo nca Inu, koma kwa ife manyazi a nkhope yathu, monga lero lino; kwa anthu a Yuda, ndi kwa okhala m'Yerusalemu, ndi kwa Aisrayeli onse okhala pafupi ndi okhala kutali, ku maiko onse kumene mudawaingira, cifukwa ca kulakwa kwao anakulakwirani nako.

8. Ambuye, kwa ife kuli manyazi a nkhope yathu, kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, ndi kwa makolo athu; pakuti takucimwirani.

9. Ambuye Mulungu wathu ndiye wacifundo, ndi wokhululukira; pakuti tampandukira Iye;

10. sitinamvera mau a Yehova Mulungu wathu, kuyenda m'malamulo ace anatiikirawo pamaso pathu, mwa atumiki ace aneneri.

11. Inde Israyeli yense walakwira cilamulo canu, ndi kupambuka, kuti asamvere mau anu; cifukwa cace temberero lathiridwa pa ife, ndi Ilumbiro lolembedwa m'cilamulo ca Mose mtumiki wa Mulungu; pakuti tamcimwira.

Werengani mutu wathunthu Danieli 9