Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 9:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo pakunena ine, ndi kupemphera, ndi kubvomereza cimo langa, ndi cimo la anthu amtundu wanga Israyeli, ndi kutula cipembedzero canga pamaso pa Yehova Mulungu wanga, cifukwa ca phiri lopatulika la Mulungu wanga;

21. inde pakunena ine m'kupemphera, munthu uja Gabrieli, amene ndidamuona m'masomphenya poyamba paja, anauluka mwaliwiro nandikhudza ngati nthawi yakupereka nsembe ya madzulo.

22. Ndipo anandilangiza ine, ndi kulankhula nane, nati, Danieli iwe, ndaturuka tsopano ine kukuzindikiritsa mwaluntha.

23. Pakuyamba iwe mapembedzero ako, linaturuka lamulo; ndipo ndadza ine kukufotokozera; pakuti ukondedwa kwambiri; zindikira tsono mau awa, nulingirire masomphenyawo.

Werengani mutu wathunthu Danieli 9