Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 8:9-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo mu imodzi ra izi munaphuka nyanga yaing'ono, imene inakula kwakukuru ndithu, kuloza kumwela, ndi kum'mawa, ndi ku dziko lokometsetsa.

10. Nikula, kufikira khamu la kuthambo; ndi zina za khamulo ndi za nyenyezi inazigwetsa pansi, nizipondereza.

11. Inde inadzikulitsa kufikira kwa kalonga wa khamulo, nimcotsera nsembe yopsereza yacikhalire; ndi pokhala malo ace opatulika panagwetsedwa.

12. Ndipo khamulo linaperekedwa kwa iyo, pamodzi ndi nsembe yopsereza yacikhalire mwa kulakwa kwace, nigwetsa pansi coonadi, nicita cifuniro cace, nikuzika.

Werengani mutu wathunthu Danieli 8