Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 8:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pamenepo ndinamva wina woyera, alikunena; ndi wina woyera anati kwa iye uja wanenayo, Masomphenya a nsembe yopsereza yacikhalire, ndi colakwa cakupululutsa ca kupereka malo opatulika ndi khamulo ziponderezedwe, adzakhala mpaka liti?

14. Nati kwa ine, Mpaka masiku zikwi ziwiri mphambu mazana atatu usana ndi usiku; pamenepo malo opatulika adzayesedwa olungama.

15. Ndipo kunali, nditaona masomphenyawo, ine Danieli ndinafuna kuwazindikira; ndipo taonani, panaima popenyana ndi ine ngati maonekedwe a munthu.

16. Ndipo ndinamva mau a munthu pakati pa magombe a Ulai, naitana, nati, Gabrieli, zindikiritsa munthuyu masomphenyawo.

17. Nayandikira iye poima inepo; atadza iye tsono ndinacita mantha, ndinagwa nkhope pansi; koma anati kwa ine, Zindikira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti masomphenyawo anena za nthawi ya cimariziro.

18. Ndipo m'mene analikulankhula ndi ine ndinagwidwa ndi tulo tatikuru, nkhope yanga pansi; koma anandikhudza, nandiimiritsa pokhala inepo,

19. Ndipo anati, Taona, ndidzakudziwitsa cimene cidzacitika pa citsiriziro ca mkwiyowo; pakuti pa nthawi yoikika mpakutha pace,

Werengani mutu wathunthu Danieli 8