Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 7:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka coyamba ca Belisazara mfumu ya ku Babulo Danieli anaona loto, naona masomphenya a m'mtima mwace pakama pace; ndipo analemba lotolo, nalifotokozera, mwacidule.

2. Danieli ananena, nati, Ndinaona m'masomphenya anga usiku, taonani, mphepo zinai za mumlengalenga zinabuka pa nyanja yaikuru.

3. Ndipo zinaturuka m'nyanja zirombo zazikuru zinai zosiyana-siyana.

4. Coyamba cinanga mkango, cinali nao mapiko a ciombankhanga, ndinapenyera mpaka nthenga zace zinathothoka, nicinakwezeka kudziko, ndi kuimitsidwa ndi mapazi awiri ngati munthu, nicinapatsidwa mtima wa munthu.

5. Ndipo taonani, cirombo cina caciwiri cikunga cimbalangondo cinatundumuka mbali imodzi; ndi m'kamwa mwace munali nthiti zitatu pakati pa mano ace; ndipo anatero naco, Nyamuka, lusira nyama zambiri.

6. Pambuyo pace ndinapenya ndi kuona cina ngati nyalugwe, cinali nao mapiko anai a nkhuku pamsana pace, ciromboco cinali nayonso mitu inai, nicinapatsidwa ulamuliro.

7. Pambuyo pace ndinaona m'masomphenya a usiku, ndi kuona cirombo cacinai, coopsa ndi cocititsa mantha, ndi camphamvu coposa, cinali nao mano akuru acitsulo, cinalusa ndi kuphwanya ndi kupondereza cotsala ndi mapazi ace; cinasiyana ndi zirombo zonse zidacitsogolera; ndipo cinali ndi nyanga khumi.

8. Ndinali kulingirira za nyangazi, taonani, pakati pa izo panaphuka nyanga yina, ndiyo yaing'ono; patsogolo pace zitatu za nyanga zoyambazi zinazulidwa ndi mizu yomwe; ndipo taonani, m'nyanga m'menemo munali maso ngati maso a munthu, ndi pakamwa palikunena zazikuru.

Werengani mutu wathunthu Danieli 7