Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 4:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. umene masamba ace anali okoma, ndi zipatso zace zocuruka, ndi m'menemo munali cakudya cofikira onse, umene nyama za kuthengo zinakhala pansi pace, ndi mbalame za m'mlengalenga zinapeza pokhala pao pa nthambi yace;

22. ndinu, mfumu; mwakula, mwalimba, pakuti ukulu wanu wakula, nufikira kumwamba, ndi ufumu wanu ku cilekezero ca dziko lapansi.

23. Tsono, kuti mfumu inaona mthenga woyera wotsika kumwamba, ndi kuti, Likhani mtengowo ndi kuuononga, koma siyani citsa cace ndi mizu m'nthaka, comangidwa ndi mkombero wa citsulo ndi mkuwa, mu msipu wa kuthengo, nicikhale cokhathamira ndi mame a kumwamba, ndi gawo lace likhale pamodzi ndi nyama za kuthengo, mpaka zitampitira nthawi zisanu ndi ziwiri;

24. kumasulira kwace ndi uku, mfumu; ndipo cilamuliro ca Wam'mwambamwamba cadzera mbuye wanga mfumu:

25. kuti adzakuingitsani kukucotsani kwa anthu, ndi pokhala panu padzakhala pamodzi ndi nyama za kuthengo; ndipo mudzadya udzu ngati ng'ombe, nimudzakhala wokhathamira ndi mame a kumwamba, nizidzakupitirani nthawi zisanu ndi ziwiri, mpaka mudzadziwa kuti Wam'mwambamwamba alamulira m'ufumu wa anthu, naupereka kwa ali yense Iye afuna mwini.

Werengani mutu wathunthu Danieli 4