Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 2:7-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Nabwerezanso iwo kuyankha, nati, Mfumu ifotokozere anyamata ace lotoli, ndipo tidzaidziwitsa kumasulira kwace.

8. Mfumu inayankha, niti, Ndidziwatu kuti mukunkhuniza dala, pakuona inu kuti cinthuci candicokera.

9. Koma mukapanda kundidziwitsa lotoli, mlandu wanu ndi umodzi; popeza mwapanganiranatu mau onama ndi oipa, kuwanena pamaso panga, mpaka idzasanduka nyengo; cifukwa cace mundifotokozere lotoli, momwemo ndidzadziwa kuti mudzandidziwitsa kumasulira kwace komwe.

10. Akasidi anayankha pamaso pa mfumu, nati, Palibe munthu pa dziko lapansi wokhoza kuulula mlandu wa mfumu; cifukwa cace palibe mfumu, mkuru, kapena wolamulira, wafunsira cinthu cotere kwa mlembi, kapena wopenduza, kapena Akasidi ali onse.

11. Pakuti cinthu acifuna mfumu ncapatali; ndipo palibe wina wokhoza kuciulula pamaso pa mfumu, koma milungu imene kwao sikuli pamodzi ndi anthu.

12. Cifukwa cace mfumu inakwiya, nizaza kwambiri, nilamulira kuti awaphe anzeru onse m'Babulo.

13. M'mwemo cilamuliroco cidamveka, ndi eni nzeru adati aphedwe; anafuna-funanso Danieli ndi anzace aphedwe.

14. Pamenepo Danieli anabweza mau a uphungu wanzeru kwa Arioki mkuru wa olindirira a mfumu, adaturukawo kukapha eni nzeru a ku Babulo;

15. anayankha nati kwa Arioki mkuru wa olindirira a mfumu, Cilamuliro ca mfumu cifulumiriranji? Pamenepo Arioki anadziwitsa Danieli cinthuci.

16. Nalowa Danieli, nafunsa mfumu amuikire nthawi, kuti aululire mfumu kumasulira kwace.

17. Pamenepo Danieli anapita ku nyumba kwace, nadziwitsa anzace Hananiya, Misaeli, ndi Azariya, cinthuci;

18. kuti apemphe zacifundo kwa Mulungu wa Kumwamba pa cinsinsi ici; kuti Danieli ndi anzace asaonongeke pamodzi ndi eni nzeru ena a ku Babulo.

Werengani mutu wathunthu Danieli 2