Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 2:26-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Mfumu inayankha, niti kwa Danieli, amene dzina lace ndiye Belitsazara, Ukhoza kodi kundidziwitsa lotolo ndidalilota, ndi kumasulira kwace?

27. Nayankha Danieli pamaso pa mfumu, nati, Cinsinsi inacitira liuma mfumu, angakhale anzeru, openduza, alembi, kapena alauli, sakhoza kuciululira mfumu;

28. koma kuli Mulungu Kumwamba wakubvumbulutsa zinsinsi; Iye ndiye wadziwitsa mfumu Nebukadinezara cimene cidzacitika masiku otsiriza. Loto lanu, ndi masomphenya a m'mtima mwanu pakama panu, ndi awa:

29. Inu mfumu, maganizo anu analowa m'mtima mwanu muli pakama panu, akunena za ico cidzacitika m'tsogolomo; ndipo Iye amene abvumbulutsa zinsinsi wakudziwitsani codzacitikaco.

30. Koma ine, cinsinsi ici sicinabvumbulutsidwa kwa ine cifukwa ca nzeru ndiri nayo yakuposa wina ali yense wamoyo, koma kuti kumasuliraku kudziwike kwa mfumu, ndi kuti mudziwe maganizo a mtima wanu.

31. Inu mfumu munapenya ndi kuona fano lalikuru. Fanoli linali lalikuru, ndi kunyezimira kwace kunaposa; linali kuima popenyana ndi inu, ndi maonekedwe ace anali oopsa,

32. Pano ili tsono, mutu wace unali wagolidi wabwino, cifuwa cace ndi manja ace zasiliva, mimba yace ndi cuuno cace zamkuwa,

33. miyendo yace yacitsulo, mapazi ace mwina citsulo mwina dongo.

34. Munali cipenyere kufikira mwala unasemedwa popanda manja, umene unagunda fanoli pa mapazi ace okhala citsulo ndi dongo, nuwaphwanya.

35. Pamenepo citsulo, dongo, mkuwa, siliva, ndi golidi, zinapereka pamodzi, nizinasanduka ngati mungu wa pa madwale a malimwe; ndi mphepo inaziuluza, osapezekanso malo ao; ndi mwala udagunda fanowo unasanduka phiri lalikuru, nudzaza dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Danieli 2