Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 11:27-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo mafumu awa onse awiri mitima yao idzakumbuka kucita zoipa, nadzanena bodza ali pa gome limodzi; koma osapindula nalo; pakuti kutha kwace kudzakhala pa nthawi yoikika.

28. Ndipo adzabwerera ku dziko lace ndi cuma cambiri; ndi mtima wace udzatsutsana ndi cipangano copatulika, nadzacita cifuniro cace, ndi kubwerera ku dziko lace.

29. Pa nthawi yoikika adzabwera, nadzalowa kumwela; koma sikudzakhala monga nthawi yoyamba ija, kapena yotsirizayi.

30. Pakuti zombo za ku Kitimu zidzafika kuyambana naye; cifukwa cace adzatenga nkhawa, nadzabwerera, nadzaipidwa mtima ndi cipangano copatulika, nadzacita cifuniro cace; adzabweranso, nadzasamalira otaya cipangano copatulika.

31. Ndipo ankhondo adzamuimirira, nadzadetsa malo opatulika ndi linga lace; nadzacotsa nsembe yosalekezayo, nadzaimitsa conyansa copululutsaco.

32. Ndipo akucitira coipa cipanganoco iye adzawaipsa, ndi kuwasyasyalika; koma anthu akudziwa Mulungu wao adzalimbika mtima, nadzacita mwamphamvu.

33. Ndipo aphunzitsi a anthu adzalangiza ambiri, koma adzagwa ndi lupanga, ndi lawi lamoto, ndi undende, ndi kufunkhidwa masiku ambiri.

34. Ndipo pakugwa iwo adzathandizidwa ndi thandizo laling'ono; koma ambiri adzaphatikizana nao ndi mau osyasyalika.

35. Nadzagwa aphunzitsi ena kuwayesa ndi moto, ndi kuwatsutsa, ndi kuwayeretsa, mpaka nthawi ya citsiriziro; pakuti kukaliko kufikira nthawi yoikika.

36. Ndipo mfumu idzacita monga mwa cifuniro cace, nidzadzikweza, ndi kudzikuza koposa milungu iri yonse nidzanena zodabwiza pa Mulungu wa milungu, nidzapindula, mpaka udzacitidwa ukaliwo; pakuti cotsimikizika m'mtimaco cidzacitika.

37. Ndipo sidzasamalira milungu ya makolo ace, kapena coikhumba akazi, kapena kusamalira milungu iri yonse; pakuti idzadzikuza koposa onse.

38. Koma kumalo kwace idzacitira ulemu mulungu wa malinga; ndi mulungu amene makolo ace sanaudziwa, adzaulemekeza ndi golidi, ndi siliva, ndi miyala ya mtengo wace, ndi zinthu zofunika.

39. Ndipo adzacita molimbana ndi malinga olimba koposa, pomthandiza mulungu wacilendo; ali yense wombvomereza adzamcurukitsira ulemu, nadzawacititsa ufumu pa ambiri, nadzagawa dziko mwa mtengo wace.

Werengani mutu wathunthu Danieli 11