Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 7:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Iye adzamangira dzina langa nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa cimpando ca ufumu wace ku nthawi zonse.

14. Ndidzakhala atate wace, iye nadzakhala mwana wanga; akacita coipa ndidzamlanga ndi ndodo ya anthu, ndi mikwapulo ya ana a anthu;

15. koma cifundo canga sicidzamcokera iye, monga ndinacicotsera Sauli amene ndinamcotsa pamaso pako.

16. Ndipo nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhazikikadi ku nthawi zonse pamaso pako; mpando wacifumu wako udzakhazikika ku nthawi zonse.

17. Monga mwa mau onse awa ndi monga mwa masomphenya onse awa, momwemo Natani analankhula ndi Davide.

18. Pomwepo Davide mfumu analowa, nakhalapansi pamaso pa Yehova; nati, Ine ndine yani, Yehova Mulungu, ndi banja langa ndi ciani kuti munandifikitsa pano?

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 7