Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 4:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo Jonatani mwana wa Sauli, anali ndi mwana wamwamuna wopunduka mapazi, Iyeyu anali wa zaka zisanu muja inamveka mbiri ya Sauli ndi Jonatani yocokera ku Jezreeli; ndipo mlezi wace adamnyamula nathawa; ndipo kunali pofulumira kuthawa, iye anagwa nakhala wopunduka. Dzina lace ndiye Mefiboseti.

5. Ndipo Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti, anamuka, nafika ku nyumba ya Isiboseti potentha dzuwa popumula iye usana.

6. Ndipo iwo analowanso kufikira m'kati mwa nyumba, monga ngati anadzatenga tirigu; namgwaza m'mimba mwace; ndi Rekabu ndi Baana mbale wace anathawa.

7. Koma polowa iwo m'nyumbamo iye ali cigonere pakama pace m'cipindamo, anamkantha, namupha namdula mutu wace, nautenga namuka njira ya kucidikha usiku wonse,

8. Ndipo anabwera nao mutu wa Isiboseti kwa Davide ku Hebroni, nanena ndi mfumu, Taonani mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu amene anafuna moyo wanu; Yehova anabwezerera cilango mbuye wanga mfumu lero lino kwa Sauli ndi mbeu yace.

9. Ndipo Davide anayankha Rekabu ndi Baana mbale wace, ana a Rimoni wa ku Beeroti, nanena nao, Pali Yehova amene anaombola moyo wanga m'masautso onse,

10. muja munthu wina anandiuza kuti, Onani Sauli wamwalira, ndi kulingalira kuti alikubwera nao uthenga wabwino, ndinamgwira ndi kumupha ku Zikilaga, ndiyo mphotho yace ndinampatsa cifukwa ca uthenga wace.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 4