Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 23:4-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Iye adzakhala ngati kuunika kwa m'mawa, poturuka dzuwa,M'mawa mopanda mitambo;Pamene msipu uphuka kuturuka pansi,Cifukwa ca kuwala koyera, italeka mvula.

5. Zoonadi nyumba yanga siikhala yotere ndi Mulungu;Koma iye anapangana ndi ine pangano losatha,Lolongosoka mwa zonse ndi losungika;Pakuti ici ndi cipulumutso canga conse, ndi kufuma kwanga konse,Kodi sadzacimeretsa?

6. Koma oipa onse adzakhala ngati minga yoyenera kuitaya,Pakuti siigwiridwa ndi dzanja;

7. Koma wakukhudza iyo adzikonzeratu citsulo ndi luti la mkondo;Ndipo idzatenthedwa konse ndi mota m'malo mwao.

8. Maina a ngwazi Davide anali nazo ndiwo: Josebu-basebete Mtakemoni, mkuru wa akazembe; ameneyu ndiye Adino M-ezni wolimbana ndi mazana atatu ophedwa nthawi imodzi.

9. Ndipo wotsatana naye Eleazeri mwana wa Dodai mwana wa M-akohi, mmodzi wa ngwazi zitatu zokhala ndi Davide pamene iwo anatonza Afilisti osonkhanidwa kunkhondo kumeneko, atacoka Aisrayeli;

10. iye ananyamuka, nakantha Afilisti kufikira dzanja lace linalema, ndi dzanja lace lomamatika kulupanga; ndipo Yehova anacititsa cipulumutso cacikuru tsiku lija, ndipo anthu anabwera m'mbuyo mwace kukafunkha kokha.

11. Ndipo wotsatana naye ndiye Sama mwana wa Age Mharario Ndipo Afilisti anasonkhana ali gulu pamene panali munda wamphodza; anthu nathawa Afilistiwo.

12. Koma iyeyoanaima pakati pa mundawo, naucinjiriza, napha Afilistiwo. Ndipo Yehova anacititsa cipulumutso cacikuru.

13. Ndipo atatu a mwamakumi atatu opambanawo, anatsika nafika kwa Davide nyengo ya kukolola m'phanga la ku Adulamu; ndi gulu la Afilisti Gnamanga zithando m'cigwa ca Refaimu.

14. Pamenepo Davide anali m'linga, ndi boma la Afilisti linali m'Betelehemu.

15. Ndipo Davide analakalaka nati, Ha! wina akadandipatsa madzi a m'citsime ca ku Betelehemu ciri pacipatapo!

16. Ndipongwazi zitatuzo zinapyola khamu la Afilisti, nizitunga madzi m'citsime ca ku Betelehemu, ca pa cipataco, nawatenga, nafika nao kwa Davide; koma iye sanafuna kumwako, koma anawathira pansi kwa Yehova.

17. Nati, Ndisacite ici ndi pang'ono ponse, Yehova; ndimwe kodi mwazi wa anthu awa ana pitawa ndi kutaya moyo wao? Cifukwa cace iye anakana kumwa. Izi anazicita ngwazi zitatuzi.

18. Ndipo Abisai, mbale wa Yoabu, mwana wa Zeruya, anali wamkuru wa atatuwa. Iye natukula mkondo wace pa anthu mazana atatu nawapha, natenga dzina iye mwa atatuwa.

19. Kodi iye sindiye waulemu mwa atatuwa? cifukwa cace anali kazembe wao; ngakhale iyenso sadafikana ndi atatu oyamba.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 23