Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 21:12-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Davide ananka natenga mafupa a Sauli ndi mafupa a Jonatani mwana wace kwa anthu a ku Jabezi Gileadi amene anawaba m'khwalala la Betisani, kumene Afilisti adawapacika, tsiku lija Afilistiwo anapha Sauli ku Giliboa;

13. nacotsa kumeneko mafupa a Sauli ndi mafupa a Jonatani mwana wace; nasonkhanitsa iwo mafupa a iwo aja adapacikidwa.

14. Naika mafupa a Sauli ndi Jonatani mwana wace ku dziko la Benjamini m'Zela, m'manda a Kisi atate wace; nacita zonse inalamulira mfumu. Ndipo pambuyo pace Mulungu anapembedzeka za dzikolo.

15. Ndipo Afilisti anaponyananso nkhondo ndi Aisrayeli; ndipo Davide anatsika ndi anyamata ace pamodzi naye naponyana ndi Afilisti; nafuna kukomoka Davide.

16. Ndipo Isibenobi, ndiye wa ana a Rafa, amene kulemera kwa mkondo wace kunali masekeli mazana atatu a mkuwa, iyeyo anabvala lupanga latsopano, nati aphe Davide.

17. Koma Abisai mwana wa Zeruya anamthandiza namkantha Mfliistiyo, namupha. Pomwepo anthu a Davide anamlumbirira iye nati, Inu simudzaturuka nafenso kunkhondo, kuti mungazime nyali ya Israyeli.

18. Ndipo kunali citapita ici, kunalinso nkhondo ndi Afilisti ku Gobu; pamenepo Sibekai Mhusati anapha Safi, ndiye wa ana a Rafa.

19. Ndipo panalinso nkhondo ndi Afilisti ku Gobu; ndipo Elhanani mwana wa Jare-oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliate Mgiti, amene mtengo wa mkondo wace unanga mtanda wa woombera nsaru.

20. Ndipo panalinso nkhondo ku Gati, kumene kunali munthu wa msinkhu waukuru, amene anali nazo zala zisanu ndi cimodzi pa dzanja lonse, ndi pa phazi lonse zala zisanu ndi cimodzi kuwerenga kwa zonse ndiko makumi awiri ndi zinai; ndipo iyenso anambala ndi Rafa.

21. Ndipo pakutonza Israyeli iyeyu, Jonatani mwana wa Simeyi mbale wa Davide anamupha.

22. Awa anai anawabala ndi Rafa, ku Gati; ndipo anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ace.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 21