Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 18:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo Yoabu analiza lipenga, ndipo anthu anabwerera naleka kupitikitsa Aisrayeli; pakuti Yoahu analetsa anthuwo.

17. Ndipo anatenga Abisalomu namponya m'cidzenje cacikuru kunkhalangoko; naunjika pamwamba pace mulu waukuru ndithu wamiyala; ndipo Aisrayeli onse anathawa yense ku hema wace.

18. Koma Abisalomu akali moyo adatenga nadziutsira coimiritsaco ciri m'cigwa ca mfumu; pakuti anati, Ndiribe mwana wamwamuna adzakhala cikumbutso ca dzina langa; nacha coimiritsaco ndi dzina la iye yekha; ndipo cichedwa cikumbutso ca Abisalomu, kufikira lero lomwe.

19. Pomwepo Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, Ndithamange nditengere mfumu mau kuti Yehova wabwezera cilango adani ace.

20. Ndipo Yoabu ananena naye, Sudzakhala iwe wotengera mau lero, koma tsiku lina udzatengera mau; koma lero sudzatengera mau, cifukwa mwana wa mfumu wafa.

21. Pamenepo Yoabu ananena ndi Mkusi, Kauze mfumu zimene unaziona. Ndipo Mkusi anawerama kwa Yoabu, nathamanga.

22. Ndipo Ahimaazi mwana wa Zadoki ananena kaciwiri kwa Yoabu, Komatu, mundilole ndithamange inenso kutsata Mkusi. Ndipo Yoabu anati, Udzathamangiranji, mwana wanga, popeza sudzalandira mphotho ya pa mauwo?

23. Koma ngakhale kotero, anati iye, Ndithamange, iye nanena naye, Thamanga. Ndipo Ahimaazi anathamanga njira ya kucigwa, napitirira Mkusi.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 18