Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 16:9-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pomwepo Abisai mwana wa Zeruya ananena ndi mfumu, Garu wakufa uyu atukwaniranji mbuye wanga mfumu? Mundilole ndioloke ndi kudula mutu wace.

10. Mfumu niti, Ndiri ndi ciani ndi inu, ana a Zeruya? Pakuti atukwana, ndi pakuti Yehova ananena naye, Utukwane Davide; ndani tsono adzanena, Watero cifukwa ninji?

11. Ndipo Davide ananena ndi Abisai ndi anyamata ace onse, Onani, mwana wanga woturuka m'matumbo anga, alikufuna moyo wanga; koposa kotani nanga Mbenjamini uyu? mlekeni, atukwane, pakuti Yehova anamuuza.

12. Kapena Yehova adzayang'anira cosayeneraci alikundicitira ine, ndipo Yehova adzandibwezera cabwino m'malo mwa kunditukwana kwa lero.

13. Comweco Davide ndi anthu ace anapita m'ngra, ndipo Simeyi analambalala paphiri popenyana naye, namuka natukwana, namponya miyala, nawaza pfumbi,

14. Ndipo mfumu ndi anthu onse amene anali naye anafika olema; ndipo iye anadzitsitsimutsa kumeneko.

15. Ndipo Abisalomu, ndi anthu onse amuna a Israyeli, anafika ku Yerusalemu, ndi Ahitofeli pamodzi naye.

16. Ndipo kunali pakudza kwa Abisalomu Husai M-ariki, bwenzi la Davide, Husai ananena ndi Abisalomu, Mfumu ikhale ndi moyo, Mfumu ikhale ndi moyo.

17. Ndipo Abisalomu ananena ndi Husai, Kodi cimeneci ndi cifundo cako ca pa bwenzi lako? unalekeranji kupita ndi bwenzi lako?

18. Husai nanena ndi Abisalomu, lai; koma amene Yehova anasankha ndi anthu awa, ndi anthu onse a Israyeli, ine ndiri wace, ndipo ndidzakhala naye iyeyu.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 16