Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 15:28-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ona ndidzaima pa madooko a m'cipululu kufikira afika mau ako akunditsimikizira ine.

29. Cifukwa cace Zadoki ndi Abyatara ananyamulanso likasa la Mulungu nafika nalo ku Yerusalemu. Ndipo iwo anakhala kumeneko.

30. Ndipo Davide anakwera pa cikweza ca ku Azitona nakwera nalira misozi; ndipo anapfunda mutu wace nayenda ndi mapazi osabvala; ndi anthu onse amene anali naye anapfunda munthu yense mutu wace, ndipo anakwera, nalira misozi pokwerapo.

31. Ndipo wina anauza Davide nati, Ahitofeli ali pakati pa opangana ciwembu pamodzi ndi Abisalomu. Davide nati, Yehova, musandulize uphungu wa Ahitofeli ukhale wopusa.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 15