Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 15:10-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Koma Abisalomu anatumiza ozonda ku mafuko onse a Israyeli, kuti, Pakumva kulira kwa lipenga, pomwepo muzinena, Abisalomu ali mfumu ku Hebroni.

11. Ndipo pamodzi ndi Abisalomu panapita anthu mazana awiri a ku Yerusalemu ndiwo oitanidwa, namuka m'kupulukira kwao, osadziwa kanthu.

12. Ndipo Abisalomu anaitana Ahitofeli Mgiloni, mphungu wa Davide, ku mudzi wace ndiwo Gilo, pamene iye analikupereka nsembe. Ndipo ciwembuco cinali colimba; pakuti anthu anacurukacurukabe kwa Abisalomu.

13. Ndipo mthenga unafika kwa Davide nuti, Mitima ya anthu a Israyeli itsata Abisalomu.

14. Ndipo Davide ananena nao anyamata ace onse akukhala naye ku Yerusalemu, Nyamukani tithawe, tikapanda kuthawa palibe mmodzi wa ife adzapulumuka Abisalomu; fulumirani kucoka, angatipeze msanga ndi kutigwetsera zoipa ndi kukantha mudzi ndi lupanga lakuthwa.

15. Ndipo anyamata a mfumu ananena kwa mfumu, Onani, monga mwa zonse mbuye wathu mfumu adzasankha, anyamata anu ndife.

16. Mfumu nituruka, ndi banja lace lonse tinamtsata. Ndipo mfumu inasiya akazi khumi ndiwo akazi ang'ono, kusunga nyumbayo.

17. Ndipo mfumu inaturuka, ndi anthu onse anamtsata; naima ku nyumba ya payokha.

18. Ndipo anyamata ace onse anapita naye limodzi; ndi Akereri ndi Apeleti, ndi Agiti onse, anthu mazana asanu ndi limodzi omtsata kucokera ku Gati, anapita pamaso pa mfumu.

19. Pomwepo mfumu inanena kwa Itai Mgiti, Bwanji ulikupita nafe iwenso? Ubwerere nukhale ndi mfumu; pakuti uli mlendo ndi wopitikitsidwa; bwerera ku malo a iwe wekha.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 15