Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 15:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, citapita ici Abisalomu anadzikonzera gareta ndi akavalo ndi anthu makumi asanu akuthamanga momtsogolera.

2. Ndipo Abisalomu analawirira, nakaima pa njira ya kucipata; ndipo kunatero, pakakhala munthu ali yense ndi mrandu woyenera kufika kwa mfumu kuti aweruze, Abisalomu anamuitana, nati, Ndinu wa ku mudzi uti? Ndipo anati, Mnyamata wanu; ndiye wa pfuko tina la Aisrayeli.

3. Abisalomu nanena naye, Ona zokamba zako ndizo zabwino ndi zolungama; koma mfumu sinauze wina kuti adzamve za iwe.

4. Abisalomu anatinso, Mwenzi atandiika ine ndikhale woweruza m'dzikomo, kuti munthu yense amene ali ndi mrandu wace kapena cifukwa cace, akadafika kwa ine; ndipo ndikadamcitira zacilungamo!

5. Ndipo kunatero kuti pakusendera munthu ali yense kudzamlambira, iye anatambasula dzanja lace, namgwira, nampsompsona.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 15