Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 1:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. NDIPO kunali atamwalira Sauli, pamene Davide anabwera atawapha Aamaleki, ndipo Davide atakhala ku Zikilaga masiku awiri;

2. pa tsiku lacitatu, onani, munthu anaturuka ku zithando za Sauli, ali ndi zobvala zace zong'ambika, ndi dothi pamutu pace; ndipo kunatero kuti iye, pofika kwa Davide, anagwa pansi namgwadira.

3. Ndipo Davide ananena naye, Ufumira kuti iwe? iye nanena naye, Ndapulumuka ku zithando za Israyeti.

4. Ndipo Davide ananena naye, Kunaonekanji? undiuze. Nayankha iye, Anthu anathawa kunkhondo, ndipo ambiri anagwa nafa; ndipo Sauli ndi Jonatani mwana wace anafanso.

5. Ndipo Davide ananena ndi mnyamata wakumuuza, Udziwa bwang kuti Sauli ndi Jonatani mwana wace anafa?

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 1